Madzi ndi ofunika kwambiri pa moyo komanso ulimi. Zinthu ziwiri zomwe zimakhudza madzi ndi: kapezedwe ka madzi ndi kasamalilidwe ka madziwo. Kapezedwe ka madzi katha kukwezedwa kudzera mukusunga madzi pa banja kapena mudzi.Kapezedwe ka madzi kamakwezedwanso kudzera mukugwiritsa ntchito madzi mosamala kuti asathe mwamsanga; izi zimatheka kudzera mukugwiritsa ntchito madziwo kangapo.
Ndondomekozi zikulongosola njira za kagwiritsidwe ntchito ka madzi mosamala komanso kugwiritsa ntchito kangapo, kusonkhanitsa madzi a mvula ndi kasungidwe kake, kalowedwe ka madzi pansi pa nthaka, madamu ang’onoang’ono, ndi ulimi wothirira wa m’masikimu. Kapezedwe ka madzi, kangapangitse kuti madzi azisamalidwa moyenera, zomwe ndizothandiza kwa anthu onse komanso pa gwero la madzilo.