Anthu amadalira zachilengedwe kuti apeze ndalama zowathandiza pa moyo wawo. Kugwiritsa ntchito zachilengedwe mosasamala kumachittsa kuti izozi zitheretu. Choncho zachilengedwe zifunika kuzisamalira ndi kuzigwiritsa ntchito mosinira kuti phindu lomwe timapeza ku zachilengedwezo likhale lochuluka kwinaku zikugwira ntchito zake. Nkhalango zachilengedwe, malo osodza nsomba ndi madambo ndi zinthu zofunika kwambiri ndipo ziyenera kusamalidwa mosalekeza; chimodzimodzinso zomera zachilendo zitha kukhala zaphindu koma zifunika kuziyang’anira bwino popewa kuti zingafalikire mopanda dongosolo. 

Gawo lino likuunikira pa momwe tingasamalire ndi kugwiritsa ntchito bwino zachilengedwezi.