Pofuna kuonetsetsa kuti ntchito zosamalira komwe anthu amachokera komanso ulimi wamakono ukuchitikadi, n’kofunika kuti ntchito zochitika pakhomo, kumunda ndiponso m’mudzi nazonso zizikhala zothandiza komanso zabwino.

Ntchitozi ndi monga kumanga nkhokwe zamakono, kusamalira mijigo, nazale za mbande, mitengo yobzala mwampanda, zaukhondo, njira zina zopezera moto, kugwiritsa ntchito moto moyenera, ndi kutaya zinyatsi mwadongosolo. (Check energy)